6 Anamtsalira mmodzi, ndiye mwana wace wokondedwa; potsiriza anamtuma iye kwa iwo, nanena, Adzamcitira ulemu mwana wanga.
7 Koma olima ajawo, ananena mwa iwo okha, Ameneyu ndiye wolowa nyumba; tiyeni timuphe iye, ndipo mundawu udzakhala wathu.
8 Ndipo anamtenga, namupha iye, namtaya kunja kwa munda.
9 Pamenepo mwini munda adzacita ciani? Adzafika, nadzaononga olimawo, nadzapereka mundawo kwa ena.
10 Kodi simunawerenga ngakhale lembo ili;Mwala umene anaukana omanga nyumba,Womwewu unayesedwa mutu wa pangondya:
11 Ici cinacokera kwa Ambuye, Ndipo ciri cozizwitsa m'maso mwathu?
12 Ndipo anayesa kumgwira Iye; koma anaopa khamu la anthu, pakuti anazindikira kuti Iye anakamba fanizo ili kuwatsutsa iwo; ndipo anamsiya Iye, nacoka.