16 Ndipo ophunzira anaturuka, nafika m'mzinda, napeza monga anati kwa iwo; ndipo anakonza Paskha.
17 Ndipo pofika madzulo anadza Iye pamodzi ndi khumi ndi awiriwo.
18 Ndipo pamene anaseama iwo kudya, Yesu anati, Ndithu ndinena ndi inu, Mmodzi wa inu adzandipereka Ine, ndiye wakudya ndi Ine pamodzi.
19 Anayamba iwo kukhala ndi cisoni, ndi kunena naye mmodzi mmodzi, kuti, Ndine kodi?
20 Ndipo anati kwa iwo, Mmodzi wa khumi ndi awiriwo, ndiye wakusunsa pamodzi ndi Ine m'mbale.
21 Pakuti Mwana wa munthu amukadi, monga kwalembedwa za Iye; koma tsoka munthuyo amene apereka Mwana wa munthu! Kukadakhala bwino kwa munthu ameneyo ngati sakadabadwa iye.
22 Ndipo pamene iwo analikudya, Iye anatenga mkate, ndipo pamene anadalitsa, ananyema, napereka kwa iwo, kuti, Tengani; thupi langa ndi ili.