25 Ndithu ndinena nanu, Sindidzamwanso cipatso ca mpesa, kufikira tsiku lijalo, limene ndidzamwa ico catsopano mu Ufumu wa Mulungu.
26 Ndipo atayimba nyimbo, anaturuka, namuka ku phiri la Azitona.
27 Ndipo Yesu ananena nao, Mudzakhumudwa nonsenu; pakuti kwalembedwa,Ndidzakantha mbusa, ndi nkhosa zidzamwazika.
28 Komatu nditadzauka ndidzatsogolera inu ku Galileya.
29 Koma Petro ananena naye, Angakhale adzakhumudwa onse, komatu ine iai.
30 Ndipo Yesu ananena naye, Ndithu ndinena ndi iwe, kuti lero, usiku uno, tambala asanalire kawiri, udzandikana Ine katatu.
31 Koma iye analimbitsa mau cilimbitsire, kuti, Ngakhale ndidzafa nanu, sindidzakana Inu. Ndipo onsewo anatero.