4 Ndipo ananena kwa iwo, Kodi nkuloledwa dzuwa la Sabata kucita zabwino, kapena zoipa? kupulumutsa moyo kapena kupha? Koma anakhala cete.
5 Ndipo m'mene anawaunguza ndi mkwiyo, ndi kumva cisoni cifukwa ca kuuma kwa mitima yao, ananena kwa munthuyo, Tambasula dzanja lako. Ndipo analitambasula; ndipo linacira dzanja lace.
6 Ndipo Afarisi anaturuka, ndipo pomwepo anamkhalira upo ndi Aherode, wakumuononga Iye.
7 Ndipo Yesu anacokako pamodzi ndi ophunzira ace nanka kunyanja: ndipo linamtsata khamu lalikuru la a ku Galileya, ndi aku Yudeya,
8 ndi a ku Yerusalemu, ndi a ku Idumeya, ndi a ku tsidya lina la Y ordano, ndi a kufupi ku Turo ndi Sidoni, khamu lalikuru, pakumva zazikuruzo anazicita, linadza kwa Iye.
9 Ndipo anati kwa ophunzira ace, kuti kangalawa kamlinde Iye, cifukwa ca khamulo, kuti angamkanikize Iye,
10 pakuti adawaciritsa ambiri; kotero kuti onse akukhala nazo zowawa anakanikiza Iye, kuti akamkhudze.