14 Ndipo akuziweta anathawa, nauza m'mudzi, ndi kwninda. Ndipo anadza kudzaona cocitikaco.
15 Ndipo anadza kwa Yesu, napenya wogwidwa ziwandayo alikukhala pansi, wobvala ndi wa nzeru zace zabwino, ndiye amene anali ndi legio; ndipo anaopa iwo.
16 Ndipo adapenyawo adawafotokozera umo anacitira ndi wogwidwa ziwandayo, ndi za nkhumbazo.
17 Ndipo anayamba kumpempha Iye kuti acoke m'malire ao,
18 Ndipo m'mene Iye analikulowa mungalawa, anampempha waziwanda uja kuti akhale ndi Iye.
19 Ndipo sanamlola, koma ananena naye, Muka kwanu kwa abale ako, nuwauze zinthu zazikuru anakucitira Ambuye, ndi kuti anakucitira cifundo.
20 Ndipo anamuka nayamba kulalikira ku Dekapoli zinthu zazikuru Yesu adamcitira iye; ndipo anthu onse anazizwa.