6 Ndipo pakuona Yesu kutali, anathamanga, namgwadira Iye;
7 ndipo anapfuula ndi mau olimba, nanena, Ndiri ndi ciani ine ndi Inu, Yesu Mwana wa Mulungu Wamkurukuru? Ndikulumbirirani pa Mulungu, msandizunze.
8 Pakuti ananena kwa iye, Turuka iwe, mzimu wonyansa, kwa munthuyu.
9 Ndipo anamfunsa, Dzina lako ndani? Ndipo ananena kwa Iye, Dzina langa ndine Legio; cifukwa tiri ambiri.
10 Ndipo anampempha Iye kwambiri kuti asaiturutsire kunja kwace kwa dziko.
11 Ndipo panali pamenepo gulu lalikuru la nkhumba zirinkudya kuphiri.
12 Ndipo inampempha Iye, kuti, Titumizeni ife mu nkhumbazo, kuti tilowe mu izo.