48 Ndipo pakuwaona ali kubvutidwa ndi kupalasa, pakuti mphepo inadza nikomana nao, pa uionda wacinai wa usiku Iye anadza kwa iwo, alikuyenda pamwamba pa nyanja; nati awapitirire;
49 koma iwo, pamene anamuona alikuyenda panyanja, anayesa kuti ndi mzukwa, napfuula:
50 pakuti iwo onse anamuona Iye, nanthunthumira. Koma pomwepo anawalankhula nanena nao, Limbani mtima; ndinetu, musaope,
51 Ndipo Iye anakwera, nalowa kwa iwo m'ngalawa, ndipo mphepo inaleka; ndipo anadabwa kwakukuru mwa iwo okha;
52 pakuti sanazindikira za mikateyo, kama mitima yao inauma.
53 Ndipo ataoloka iwo, anafika pamtunda ku Genesarete, nakoceza padooko.
54 Ndipo pamene anaturuka m'ngalawa anamzindikila pomwepo,