5 Ndipo Afarisi ndi alembi anamfunsa Iye, kuti, Bwanji ophunzira anu satsata mwambo wa akuru, koma akudya mkate wao ndi m'manja mwakuda?
6 Ndipo Iye ananena nao, Yesaya ananenera bwino za inu onyenga, monga mwalembedwa,Anthu awa andilemekeza Ine ndi milomo yao,Koma mtima wao ukhala kutari ndi ine.
7 Koma andilambira Ine kwacabe,Ndi kuphunzitsa maphunzitso, malangizo a anthu.
8 Musiya lamulo la Mulungu, nimusunga mwambo wa anthu.
9 Ndipo ananena nao, Bwino mukaniza lamulo la Mulungu, kuti musunge mwambo wanu,
10 Pakuti Mose anati, Lemekeza atate wako ndi amako; ndipo iye wakunenera zotpa atate wace kapena amai wace, afe ndithu;
11 koma inu munena, Munthu akati kwa atate wace, kapena amai wace, Karban, ndiko kuti Mtulo, cimene ukadathandizidwa naco ndi ine,