1 Masiku ajawo pakukhalanso khamu lalikuru la anthu, ndipo analibe kanthu kakudya, iye anadziitanira ophunzira ace, nanena nao,
2 Ndimva nalo cifundo khamulo, cifukwa ali ndi Ine cikhalire masiku atatu, ndipo alibe kanthu kakudya:
3 ndipo ngati ndiwauza iwo amuke kwao osadya kanthu, adzakomoka panjira; ndipo ena iwo acokera kutali.
4 Ndipo ophunzira ace anamyankha Iye, kuti, Munthu adzatha kutenga kuti mikate yakukhutitsa anthu awa m'cipululu muno?