3 ndipo ngati ndiwauza iwo amuke kwao osadya kanthu, adzakomoka panjira; ndipo ena iwo acokera kutali.
4 Ndipo ophunzira ace anamyankha Iye, kuti, Munthu adzatha kutenga kuti mikate yakukhutitsa anthu awa m'cipululu muno?
5 Ndipo anawafunsa, Muli nayo mikate ingati? Ndipo anati, Isanu ndi iwiri.
6 Ndipo analamulira anthu a khamulo akhale pansi; natenga mikate isanu ndi iwiriyo, nayamika, nanyema, napatsa ophunzira ace, kuti apereke kwa iwo; ndipo anapereka kwa khamulo.
7 Ndipo anali nato tinsomba towerengeka; ndipo Iye anatidalitsa, nati atipereke itonso.
8 Ndipo anadya nakhuta; ndipo anatola makombo malicero asanu ndi awiri.
9 Ndipo iwo anali ngati zikwi zinai; ndipo Iye analawirana nao.