40 Comweco mfumu inaoloka nifika ku Giligala, ndi Cimamu anaoloka naye, ndipo anthu onse a Yuda adaolotsa mfumu, ndiponso gawo lina la anthu a Israyeli.
41 Ndipo onani, Aisrayeli onse anafika kwa mfumu, nanena ndi mfumu, Abale athu anthu a Yuda anakucotsani bwanji mwakuba, naolotsa mfumu ndi banja lace pa Yordano, ndi anthu onse a Davide pamodzi naye?
42 Ndipo anthu onse a Yuda anayankha anthu a Israyeli. Cifukwa mfumu iri ya cibale cathu; tsono mulikukwiyiranji pa mrandu umenewu? tinadya konse za mfumu kodi? kapena kodi anatipatsa mtulo uli wonse?
43 Ndipo anthu a Israyeli anayankha anthu a Yuda, nati, Ife tiri ndi magawo khumi mwa mfumu, ndi mwa Davide koposa inu; cifukwa ninji tsono munatipeputsa ife, osayamba kupangana nafe za kubwezanso mfumu yathu? Koma mau a anthu a Yuda anali aukali koposa mau a anthu a Israyeli.