1 Abale, kufunitsa kwa mtima wanga ndi pemphero langa limene ndiwapempherera kwa Mulungu, ndilo, kuti apulumuke.
2 Pakuti ndiwacitira iwo umboni kuti a ali ndi cangu ca kwa Mulungu, koma si monga mwa cidziwitso.
3 Pakuti pakusadziwa cilungamo ca Mulungu, ndipo pofuna kukhazikitsa cilungamo ca iwo okha, iwo sanagonja ku cilungamo ca Mulungu.
4 Pakuti Kristu ali cimariziroca lamulo kulinga kucilungamo kwa amene ali yense akhulupira,
5 Pakuti Mose walemba kuti munthu amene acita cilungamo ca m'lamulo, adzakhala naco ndi moyo.
6 Koma cilungamo ca cikhulupiriro citero, Usamanena mumtima mwako, Adzakwera ndani Kumwambako? ndiko, kutsitsako Kristu;
7 kapena, Adzatsikira ndani kudzenieko? ndiko, kukweza Kristu kwa akufa.