26 kuti aonetse cilungamo cace m'nyengo yatsopano; kuti iye akhale wolungama, ndi wakumuyesa wolungama iye amene akhulupirira Yesu,
27 Pamenepo kudzitama kuli kuti? Kwaletsedwa. Ndi lamulo lotani? La nchito kodi? lai; koma ndi lamulo la cikhulupiriro.
28 Pakuti timuyesa munthu wohmgama cifukwa ca cikhulupiriro, wopanda nchito za lamulo.
29 Kapena Mulungu ndiye wa Ayuda okha okha kodi? si wao wa amitundunso kodi? Bya, wa amitundunso:
30 ngatitu ndiye Mulungu mmodzi, amene adzawayesa amdulidwe olungama ndi cikhulupiriro, ndi akusadulidwa mwa cikhulupiriro,
31 Potero kodi lamulo tiyesa cabe mwa cikhulupiriro? Msatero ai; koma tikhazikitsa lamulo.