30 Cifukwa cace tidzatani? 5 Kuti amitundu amene sanatsata cilungamo, anafikira cilungamo, ndico cilungamo ca cikhulupiriro;
31 6 koma Israyeli, potsata lamulo la cilungamo, sanafikira lamulolo.
32 Cifukwa canji? Cifukwa kuti sanacitsata ndi cikhulupiriro, koma monga ngati ndi nchito. 7 Anakhumudwa pa mwala wokhumudwitsa;
33 monganso kwalembedwa, kuti,8 Onani, ndikhazika m'Ziyoni mwala wakukhumudwa nao, ndi thanthwe lopunthwitsa;Ndipo 9 wakukhulupirira iye sadzacita manyazi.