16 ndipo sanalola munthu ali yense kunyamula cotengera kupyola pakati pa Kacisi.
17 Ndipo anaphunzitsa, nanena nao, Sicilembedwa kodi, Nyumba yanga idzachedwa nyumba yakupempheramo anthu a mitundu yonse? koma inu mwaiyesa phanga la acifwamba.
18 Ndipo ansembe akuru ndi alembi anamva, nafunafuna momuonongera Iye; pakuti anamuopa, cifukwa khamu lonse la anthu linazizwa ndi ciphunzitso cace.
19 Ndipo masiku onse madzulo anaturuka Iye m'mudzi.
20 Ndipo m'mene anapitapo m'mawa mwace, anaona kuti mkuyu uja unafota, kuyambira kumizu.
21 Ndipo Petro anakumbukila, nanena naye, Rabi, onani, wafota mkuyuwo munautemberera.
22 Ndipo Yesu anayankha nanena nao, Khulupirirani Mulungu,