42 Ndipo atafika tsono madzulo, popeza mpa tsiku lokonzera, ndilo la pambuyo pa Sabata,
43 anadzapo Y osefe wa ku Arimateya, mkulu wa mirandu womveka, amene yekha analikuyembekezera Ufumu wa Mulungu; nalimba mtima nalowa kwa Pilato, napempha mtembo wace wa Yesu.
44 Ndipo Pilato anazizwa ngati adamwaliradi; naitana kenturiyo, namfunsa ngati adamwalira kale.
45 Ndipo pamene anacidziwa ndi kenturiyo, anamninkha Yosefe ntembowo.
46 Ndipo anagula oafuta, namtsitsa Iye, namkulunga n'bafutamo, namuika m'manda osenedwa m'thanthwe; nakunkhunicira mwala pa khomo la manda.
47 Ndipo Maliya wa Magadala ndi Maliya amace wa Yose anapenya pomwe anaikidwapo.