33 Koma mkaziyo anacita mantha, ndi kunthunthumira, podziwa cimene anamcitira iye, nadza, namgwadira, namuuza coona conse.
34 Ndipo anati kwa iye, Mwana wamkaziwe, cikhulupiriro, cako cakupulumutsa; muka mumtendere, nukhale wocira cibvutiko cako.
35 M'mene iye ali cilankhulire, anafika a ku nyumba ya mkuru wa sunagoge, nanena, kuti, Mwana wako wafa; ubvutiranjinso Mphunzitsi?
36 Koma Yesu wosasamala mau olankhulidwawo, ananena kwa mkuru wa sunagoge, Usaope, khulupirira kokha.
37 Ndipo sanalola munthu yense kutsagana naye, koma Petro, ndi Yakobo, ndi Yohane mbale wace wa Yakobo.
38 Ndipo anafika ku nyumba kwace kwa mkuru wa sunagoge; ndipo anaona cipiringu, ndi ocita maliro, ndi akukuwa ambiri
39 Ndipo m'mene atalowa, ananena nao, Mubuma ndi kulira bwanji? Mwana sanafa, koma ali m'tulo.