34 Ndipo anadziitanira khamulo la anthu pamodzi ndi ophunzira ace, nati kwa iwo, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikanize yekha, nanyamule mtanda wace, nanditsate Ine.
35 Pakuti yense wakufuna kupulumutsa moyo wace adzautaya; ndipo yense wakutaya moyo wace cifukwa ca Ine, ndi cifukwa ca Uthenga Wabwino, adzaupulumutsa.
36 Pakuti munthu apindulanji akadzilemezera dziko lonse, natayapo moyo wace?
37 Pakuti munthu akapereka ciani cosintha naco moyo wace?
38 Pakuti yense wakucita manyazi cifukwa ca Ine, ndi ca mau anga mu mbadwo uno wacigololo ndi wocimwa, Mwana wa munthu adzacitanso manyazi cifukwa ca iyeyu, pamene Iye adzafika nao angelo ace oyera, mu ulemerero wa Atate wace.