8 Ndipo mfumu inanena ndi mkaziyo, Pita ku nyumba yako, ndipo ndidzalamulira za iwe.
9 Ndipo mkazi wa ku Tekowayo ananena ndi mfumu, Mbuye wanga mfumu, mphulupulu ikhale pa ine ndi pa nyumba ya atate wanga; ndipo mfumu ndi mpando wacifumu wao zikhale zopanda cifukwa.
10 Ndipo mfumu inati, Ubwere naye kwa ine ali yense wakunena kanthu ndi iwe, ndipo iyeyo sadzakukhudzanso.
11 Nati iye, Mfumu mukumbukile Yehova Mulungu wanu kuti wolipsa mwazi asaonjeze kuononga, kuti angaononge mwana wanga. Niti iyo, Pali Yehova, palibe tsitsi limodzi la mwana wako lidzagwa pansi.
12 Pamenepo mkaziyo anati, Mulole mdzakazi wanu alankhule mau kwa mbuye wanga mfumu. Niti Iyo, Nena.
13 Ndipo mkaziyo anati, Cifukwa ninjinso munalingalira cinthu cotere pa anthu a Mulungu? pakuti pakulankhula mau awa mfumu ikunga woparamula, popeza mfumu siitumiza okamtenganso woingidwa wace.
14 Pakuti kufa tidzafa, ndipo tiri ngati madzi otayika pansi amene sakhoza kuwaolanso; ngakhale Mulungu sacotsa moyo, koma alingalira ngra yakuti wotayikayo asakhale womtayikira iye.