1 Ndipo ndinapenya, taonani, Mwanawankhosayo alikuimirira pa phiri la Ziyoni, ndipo pamodzi ndi iye zikwi zana mphambu makumi anai kudza anai, akukhala nalo dzina lace ndi dzina la Atate wace lolembedwa pamphumi pao.
2 Ndipo ndinamva mau ocokera Kumwamba, ngati mkokomo wamadzi ambiri, ndi ngati mau a bingu lalikuru; ndipo mauamene ndinawamva anakhala ngati a azeze akuyimba azeze ao j
3 ndipo ayimba ngati nyimbo yatsopane ku mpando wacifumu, ndi pamaso pa zamoyo zinai, ndi akulu; ndipo palibe munthu anakhoza kuphunzira nyimboyi, kama zikwi zana mphambu makumi anai kudza anai, ogulidwa kucokera kudziko.
4 Iwo ndiwo amene sadetsedwa pamodzi ndi akazi; pakuti ali anamwali. Iwo ndiwo amene atsata Mwanawankhosa kulikonse amukako. Iwowa anagulidwa mwa anthu, zipatso zoundukulakwa Mulungu ndi kwa Mwanawankhosa.