Cibvumbulutso 9 BL92

Lipenga lacisanu, tsoka loyamba

1 Ndipo mngelo wacisanu anaomba, ndipo ndinaona nyenyezi yocokera kumwamba idagwa padziko; ndipo anampatsa iye cifunguliro ca dzenje la phompho.

2 Ndipo anatsegula pa dzenje la phompho; ndipo unakwera utsi woturuka m'dzenjemo, ngati utsi wa ng'anjo yaikuru; ndipo dzuwa ndi thambo zinada, cifukwa ca utsiwo wa kudzenje,

3 Ndipo m'utsimo mudaturuka dzombe padziko, ndipo analipatsa ilo mphamvu monga zinkhanira za dziko ziri ndi mphamvu.

4 Ndipo ananena kwa ilo kuti lisaipse udzu wa padziko, kapena cabiriwiri ciri conse, kapena mtengo uli wonse, koma anthu amene alibe cizindikilo ca Mulungu pamphumi pao ndiwo.

5 Ndipo anapatsa ilo mphamvu si kuti likawaphe, komatu kuti likawazunze miyezi isanu; ndipo mazunzidwe ao anali ngati mazunzidwe a cinkhanira, pamene ciluma munthu.

6 Ndipo m'masiku ajawo, anthu adzafunafuna imfa osaipeza konse; ndipo adzakhumba kumwalira, koma imfa idzawathawa.

7 Ndipo maonekedwe a dzombelo anafanana ndi akavalo okonzeka kukacita nkhondo; ndi pamitu pao ngati akorona onga agolidi, ndi pankhope pao ngati pankhope pa anthu.

8 Ndipo anali nalo tsitsi Ionga tsitsi la akazi, ndipo mano ao analingati mano a mikango.

9 Ndipo anali nazo zikopa ngati zikopa zacitsulo; ndipo mkokomo wa: mapiko ao ngati mkokomo wa agareta, a akavalo ambiri akuthamangira kunkhondo.

10 Ndipo liri nayo micira yofanana ndi ya cinkhanira ndi mbola; ndipo m'micira mwao muli mphamvu yao yakuipsa anthu miyezi isanu.

11 Ndipo linali nayo Mfumu yakulilamulira, mngelo wa phompho; dzina lace m'Cihebri Abadoni, ndi m'Cihelene ali nalo dzina Apoliyoni.

Lipenga lacisanu ndi cimodzi, tsoka laciwiri

12 Tsoka loyamba lapita; taonani, akudzanso masoka awiri m'tsogolomo.

13 Ndipo mngelo wacisanu ndi cimodzi anaomba, ndipo ndinamva mau ocokera ku nyanga za guwa la nsembe lagolidi liri pamaso pa Mulungu,

14 nanena kwa mngelo wacisanu ndi cimodzi wakukhala ndi lipenga, Masula angelo anai omangidwa pa mtsinje waukuru Pirate.

15 Ndipo anamasulidwa angelo anai, okonzeka kufikira ora ndi tsiku ndi mwezi ndi caka, kuti akaphe limodzi la magawo atatu a anthu.

16 Ndipo ciwerengero ca nkhondo za apakavalo ndico zikwi makumi awiri zocurukitsa zikwi khumi; ndinamva ciwerengero cao.

17 Ndipo kotero ndinaona akavalo m'masomphenya, ndi iwo akuwakwera akukhala nazo zikopa za moto, ndi huakinto ndi sulfure; ndi mitu ya akavalo ngati mitu ya mikango; ndipo m'kamwa mwao muturuka moto ndi utsi ndi sulfure.

18 Ndi miliri iyi linaphedwa limodzi la magawo atatu a anthu, ndi moto, ndi utsi, ndi sulfure, zoturuka m'kamwa mwao.

19 Pakuti mphamvu ya akavalo in m'kamwa mwao, ndi m'micira yao; pakuti micira yao ifanana ndi njoka, nikhala nayo mitu, ndipo aipsa nayoyo.

20 Ndipo otsala a anthu osaphedwa nayo miliri iyo sanalapa nchito ya manja ao, kuti asapembedzere ziwanda, ndi mafano agolidi, ndi asiliva, ndi amkuwa, ndi amwala, ndi amtengo, amene sakhoza kupenya, kapena kumva, kapena kuyenda;

21 ndipo sanalapa mbanda zao, kapena nyanga zao, kapena cigololo cao, kapena umbala wao.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22