2 Ndipo ndinaona mngelo wina, anakwera kucokera poturuka dzuwa, ali naco cizindikilo ca Mulungu wamoyo: ndipo anapfuula ndi mau akuru kuitana angelo anai, amene adalandira mphamvu kuipsa dziko ndi nyanja,
3 nanena, Musaipse dziko, kapena nyanja, kapena mitengo, kufikira tidasindikiza cizindikilo akapolo a Mulungu wathu, pamphumi pao.
4 Ndipo ndinamva ciwerengo ca iwo osindikizidwa cizindikilo, zikwi makumi khumi ndi makumi anai mphambu anai, osindikizidwa cizindikilo mwa mafuko onse a ana a Israyeli,
5 Mwa pfuko la Yuda anasindikizidwa cizindikilo zikwi khumi ndi ziwiri:Mwa pfuko la Rubeni zikwi khumi ndi ziwiri:Mwa pfuko la Gadi zikwi khumi ndi ziwiri:
6 Mwa pfuko la Aseri zikwi khumi ndi ziwiri:Mwa pfuko la Nafitali zikwi khumi ndi ziwiri:Mwa pfuko la Manase zikwi khumi ndi ziwiri:
7 Mwa pfuko la Simeoni zikwi khumi ndi ziwiri:Mwa pfuko la Levi zikwi khumi ndiziwiri:Mwa pfuko la Isakara zikwi khumi ndi ziwiri:
8 Mwa pfuko la Zebuloni zikwi khumi ndi ziwiri:Mwa pfuko la Yosefe zikwi khumi ndi ziwiri:Mwa pfuko la Benjamini anasindikizidwa cizindikilo zikwi khumi ndi ziwiri.