1 Ndipo ananyamuka Iye kumeneko, nadza ku maiko a ku Yudeya ndi ku tsidya lija la Yordano; ndipo anasonkhananso kwa Iye makamu a anthu; ndipo monga anazolowera, anawaphunzitsanso.
2 Ndipo anadza kwa Iye Afarisi, namfunsa Iye ngati kuloledwa kuti munthu acotse mkazi wace, namuyesa Iye.
3 Ndipo Iye anayankha nati kwa iwo, Kodi Mose anakulamulirani ciani?
4 Ndipo anati, Mose analola kulembera kalata wakulekanira, ndi kumcotsa.
5 Koma Yesu anati kwa iwo, Cifukwa ca kuuma kwa mitima yanu anakulemberani lamulo ili.