20 Ndipo anati, Coturuka mwa munthu ndico cidetsa munthu.
21 Pakuti m'kati mwace mwa mitima ya anthu, muturuka maganizo oipa, zaciwerewere,
22 zakuba, zakupha, zacigololo, masiriro, zoipa, cinyengo, cinyanso, diso loipa, mwano, kudzikuza, kupusa:
23 zoipa izi zonse zituruka m'kati, nizidetsa munthu.
24 Ndipo Iye anauka nacoka kumeneko, nanka ku maiko a ku Turo ndi Sidoni, Ndipo analowa m'nyumba, nafuna kuti asadziwe anthu; ndipo sanakhoza kubisika.
25 Koma pomwepo mkazi, kabuthu kace kanali ndi mzimu wonyansa, pamene anamva za Iye, anadza, nagwa pa mapazi ace.
26 Koma mkaziyo anali Mhelene, mtundu wace MsuroFonika. Ndipo anampempha Iye kuti aturutse ciwanda m'mwana wace.