20 Ndipo mikate isanu ndi iwiri kwa anthu zikwi zinai, munatola malicero angati odzala ndi makombo? Ndipo ananena naye, Asanu ndi awiri.
21 Ndipo Iye ananena nao, Simudziwitsa ngakhale tsopano kodi?
22 Ndipo anadza ku Betsaida. Ndipo anadza naye kwa Iye munthu wakhungu, nampempha Iye kuti amkhudze.
23 Ndipo anamgwira dzanja munthu wakhunguyo, naturukira naye kunja kwa mudzi; ndipo atamthira malobvu m'maso mwace, naika manja pa iye, anamfunsa, Uona kanthu kodi?
24 Ndipo anakweza maso, nanena, Ndiona anthu; pakuti ndiwapenya ayendayenda ngati mitengo.
25 Pamenepo anaikanso manja m'maso mwace; ndipo anapenyetsa, naciritsidwa, naona zonse mbee.
26 Ndipo anamtumiza amuke kwao, nanena, Usalowe konse m'mudzi.