2 Awa anali paciyambi kwa Mulungu,
3 Zonse: zinalengedwa ndi iye; ndipo kopanda iye sikunalengedwa kanthu kali konse kolengedwa,
4 Mwa iye munali moyo; ndi moyowu unali kuunika kwa anthu.
5 Ndipo kuunikaku kunawala mumdima; ndi mdimawu sunakuzindikira.
6 Kunali munthu, wotumidwa ndi Mulungu, dzina lace ndiye Yohane.
7 Iyeyu anadza mwa umboni kudzacita umboni za kuunikaku, kuti onse akakhulupirire mwa iye,
8 iye sindiye kuunikaku, koma anatumidwa kukacita umboni wa kuunikaku.