Yohane 12 BL92

Mariya adzoza mapazi a Yesu

1 Pomwepo anatsala masiku asanu ndi limodzi asanafike Paskha, Yesu anadza ku Betaniya kumene kunali Lazaro, amene Yesu adamuukitsa kwa akufa.

2 Ndipo anamkonzera iye cakudya komweko; ndipo Marita anatumikira; koma Lazaro anali mmodzi wa iwo akuseama pacakudya pamodzi ndi iye.

3 Pamenepo Mariya m'mene adatenga muyeso umodzi wa mafuta onunkhira bwino a nardo a mtengo wace wapatali, anadzoza mapazi a Yesu, napukuta mapazi ace ndi tsitsi lace; ndipo nyumba inadzazidwa ndi mnunkho wace wa mafutawo.

4 Koma Yudase Isikariote, mmodzi wa akuphunzira ace, amene adzampereka iye, ananena,

5 Nanga mafuta onunkhira awa sanagulitsidwa cifukwa ninji ndi marupiya atheka mazana atatu, ndi kupatsidwa kwa osauka?

6 Koma ananena ici si cifukwa analikusamalira osauka, koma cifukwa anali mbala, ndipo pokhala nalo thumba, amabazoikidwamo.

7 Pamenepo Yesu anati, Mleke iye, pakuti anacisungira ici tsiku la kuikidwa kwanga.

8 Pakuti osauka muli nao pamodzi ndi inu nthawi zonse; koma simuli ndi Ine nthawi zonse.

9 Pamenepo khamu lalikuru la Ayuda Iinadziwa kuti ali pomwepo; ndipo anadza, si cifukwa: ca Yesu yekha, koma kuti adzaone Lazaro, amene adamuukitsa kwa akufa.

10 Koma ansembe akulu anapangana kuti akaphe Lazaronso;

11 pakuti ambiri a Ayuda anacoka cifukwa ca iye, nakhulupirira Yesu.

Yesu alowa m'Yerusalemu

12 M'mawa mwace khamu lalikuru la anthu amene adadza kuphwando, pakumva kuti Yesu alinkudza ku Yerusalemu,

13 anatenga makwata a kanjedza, naturuka kukakomana ndi iye, napfuula, Hosana; wolemekezeka iye wakudza m'dzina la Ambuye, ndiye Mfumu ya Israyeli.

14 Koma Yesu, m'mene adapeza kaburu anakhala pamenepo; monga mulembedwa:

15 Usaope, mwana wamkazi wa Ziyoni; taona Mfumu yako idza wokhala pa mwana wa buru.

16 Izisanazidziwa aku phunzira ace poyamba; koma pamene Yesu analemekezedwa, pamenepo anakumbukila kuti izi zinalembedwa za iye, ndi kuti adamcitira iye izi.

17 Pamenepo khamulo limene linali pamodzi ndi iye, m'mene anaitana Lazaro kuturuka kumanda, namuukitsa kwa akufa, anacita umboni.

18 Cifukwa ca icinso khamulo linadza kudzakomana ndi iye, cifukwa anamva kuti iye adacita cizindikilo ici.

19 Cifukwa cace Afarisi ananena wina ndi mnzace, Muona kuti simupindula kanthu konse; onani dziko litsata pambuyo pace pa iye.

Ahelene afuna kuona Yesu; iye ayankhapo

20 Koma panali Ahelene ena mwa iwo akukwera kunka kukalambira paphwando,

21 Ndipo iwo anadza kwa Filipo wa ku Betsaida wa m'Galileya, namfunsa iye, ndi kuti, Mbuye, tifuna kuona Yesu.

22 Filipo anadza nanena kwa Andreya; nadza Andreya ndi Filipo, nanena ndi Yesu.

23 Koma Yesu anayankha iwo, nati, Yafika nthawi, kuti Mwana wa munthu alemekezedwe.

24 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Ngati mbeu ya tirigu siigwa m'nthaka, nifa, ikhala pa yokha iyo; koma ngati ifa, ibala cipatso cambiri.

25 Iye wokonda moyo wace adzautaya; ndipo wodana ndi moyo wace m'dziko lino lapansi adzausungira ku moyo wosatha.

26 Ngati wina anditumikira Ine, anditsate; ndipo kumene kuli Ine, komwekonso kudzakhala mtumiki wanga, Ngati wina anditumikira Ine, Atate adzamcitira ulemu iyeyu,

27 Moyo wanga wabvutika tsopano; ndipo ndidzanena ciani? Atate, ndipulumutseni Ine ku nthawi iyi. Koma cifukwa ca ici ndinadzera nthawi iyi.

28 Atate, lemekezani dzina lanu. Pomwepo adadza mau ocokera Kumwamba, ndalilemekeza, ndipo ndidzalilemekezanso.

29 Cifukwa cace khamu la anthu akuimirirako, ndi kuwamva ananena kuti kwagunda. Ena ananena, Mngelo walankhula ndi iye.

30 Yesu anayankha nati, Mau awa sanafika cifukwa ca Ine, koma ca inu.

31 Tsopano pali kuweruza kwa dziko ili lapansi; mkulu wa dziko ili lapansi adzatayidwa kunja tsopano,

32 Ndipo Ine, m'mene ndikakwezedwa kudziko, ndidzakoka anthu onse kwa Ine ndekha.

33 Koma ananena ici ndi kuzindikiritsa imfa yanji akuti adzafa nayo.

34 Pamenepo khamulo linayankha iye, Tidamva ife m'cilamulo kuti Kristu akhala ku nthawi yonse; ndipo Inu munena bwanji, kuti Mwana wa munthu ayenera kukwezedwa? Mwana wa munthu amene ndani?

35 Pamenepo Yesu anati kwa iwo, Katsala kanthawi kakang'ono ndipo kuunika kuli mwa inu. 1 Yendani pokhala muli nako kuunika, kuti mdima sungakupezeni; ndipo woyenda mumdima sadziwa kumene amukako,

36 2 Pokhala muli nako kuunika, khulupirirani kuunikako, kuti mukakhale ana a kuunikako.Izi Yesu analankhula, nacoka nawabisalira.

37 Koma angakhale adacita zizindikilo zambiri zotere pamaso pao iwo sanakhulupirira iye;

38 kuti mau a Yesaya mneneri akakwaniridwe, amene anati,3 Ambuye, wakhulupirira ndani kulalikira kwathu?Ndipo mkono wa Ambuye wabvumbulutsidwa kwa yani?

39 Cifukwa ca ici sanathe kukhulupira, pakuti Yesaya anatinso,

40 4 Wadetsa maso ao, naumitsa mtima wao;Kuti angaone ndi maso, angazindikire ndi mtima,Nangatembenuke,Ndipo ndingawaciritse.

41 5 Izi anati Yesaya, cifukwa anaona ulemerero wace; nalankhula za iye.

42 Kungakhale kotero, ambiri a mwa akuru anakhulupirira iye; koma 6 cifukwa ca Afarisi sanabvomereza, kuti angaletsedwe m'sunagoge,

43 7 pakuti anakonda ulemerero wa anthu koposa ulemerero wa Mulungu.

44 Koma Yesu anapfuula nati, 8 iye wokhulupirira ine, sakhulupirira Ine, koma iye wondituma Ine.

45 Ndipo 9 wondiona Ine aona amene anandituma Ine

46 10 Ndadza Ine kuunika ku dziko lapansi, kuti yense wokhulupirira Ine asakhale mumdima.

47 Ndipo ngati wina akumva mau anga, ndi kusawasunga, Ine sindimweruza; pakuti 11 sindinadza kudzaweruza dziko lapansi, koma kuti ndipulumutse dziko lapansi.

48 12 iye amene akaniza Ine, ndi kusalandira mau anga, ali naye womweruza iye; 13 mau amene ndalankhula, iwowa adzamweruza tsiku lomariza.

49 14 Pakuti sindinalankhula mwa Ine ndekha; koma Atate wondituma Ine, yemweyu anandipatsa Ine lamulo, limene ndikanene, ndi limene ndikalankhule.

50 Ndipo ndidziwa kuti lamulo lace liri moyo wosatha; cifukwa cace zimene ndilankhula, monga momwe Atate wanena ndi Ine, momwemo ndilankhula.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21