18 Palibe wina andicotsera uwu, koma ndiutaya Ine ndekha. Ndiri nayo mphamvu yakuutaya, ndi mphamvu ndiri nayo yakuutenganso; lamulo ili ndinalandira kwa. Atate wanga.
19 Panakhalanso kutsutsana pakati pa Ayuda cifukwa ca mau awa.
20 Koma ambiri mwa iwo ananena, Ali ndi ciwanda, nacita misala; mukumva iye bwanji?
21 Ena ananena, Mau awa sali a munthu wogwidwa ciwanda. Kodi ciwanda cikhoza kumtsegulira maso wosaona?
22 Koma kunali phwando la kukonzersanso m'Yerusalemu; nyengoyo ndi yacisanu.
23 Ndipo Yesu analikuyendayenda m'Kacisi m'khumbi la Solomo,
24 Pamenepo Ayuda anamzungulira iye, nanena ndi iye, Kufikira liti musfnkhitsa-slnkhitsa moyo wathu? ngati Inu ndinu Kristu, tiuzeni momveka.