40 4 Wadetsa maso ao, naumitsa mtima wao;Kuti angaone ndi maso, angazindikire ndi mtima,Nangatembenuke,Ndipo ndingawaciritse.
41 5 Izi anati Yesaya, cifukwa anaona ulemerero wace; nalankhula za iye.
42 Kungakhale kotero, ambiri a mwa akuru anakhulupirira iye; koma 6 cifukwa ca Afarisi sanabvomereza, kuti angaletsedwe m'sunagoge,
43 7 pakuti anakonda ulemerero wa anthu koposa ulemerero wa Mulungu.
44 Koma Yesu anapfuula nati, 8 iye wokhulupirira ine, sakhulupirira Ine, koma iye wondituma Ine.
45 Ndipo 9 wondiona Ine aona amene anandituma Ine
46 10 Ndadza Ine kuunika ku dziko lapansi, kuti yense wokhulupirira Ine asakhale mumdima.