9 za macimo, cifukwa sakhulupirira Ine;
10 za cilungamo, cifukwa ndinka kwa Atate, ndipo simundionanso;
11 za ciweruziro, cifukwa mkuru wa dziko ili lapansi waweruzidwa.
12 Ndiri nazo zambirinso zakunena kwa inu, koma simungathe kuzisenza tsopano lino.
13 Koma atadza Iyeyo, Mzimu wa coonadi, adzatsogolera inu m'coonadi conse; pakuti sadzalankhula za iye mwini; koma zinthu ziri zonse adzazimva, adzazilankhula; ndipo zinthu zirinkudza adzakulalikirani.
14 Iyeyo adzalemekeza Ine; cifukwa adzatenga za mwa Ine, nadzalalikira kwa inu.
15 Zinthu ziri zonse Atate ali nazo ndi zanga; cifukwa cace ndinati, kuti atenga za mwa Ine, nadzalalikira kwa inu.