1 Ndipo tsiku lacitatu pariali ukwati m'Kana wa m'Galileya; ndipo amace wa Yesu anali komweko.
2 Ndipo Yesu yemwe ndi akuphunzira ace anaitanidwa ku ukwatiwo.
3 Ndipo pakutha vinyo, amace wa Yesu ananena naye, Alibe vinyo,
4 Yesu nanena naye, Mkazi, ndiri ndi ciani ndi inu? nthawi yanga siinafike.