30 Anaturuka iwo m'mudzi ndipo analinkudza kwa iye.
31 Pa mphindikati iyi ophunzira ace anampempha iye, ndi kunena, Rabi, idyani.
32 Koma iye anati kwa iwo, Ine ndiri naco cakudya cimene inu simucidziwa.
33 Cifukwa cace ophunzira ananena wina ndi mnzace, Kodi pali wina anamtengera iye kanthu kakudya?
34 Yesu ananena nao, Cakudya canga ndico kuti ndicite cifuniro ca iye amene anandituma Ine, ndi kutsiriza nchito yace.
35 Kodi simunena inu, kuti, Yatsala miyezi inai, ndipo kudza kumweta? Onani ndinena kwa inu, Kwezani maso anu, nimuyang'ane m'minda, kuti mwayera kale kufikira kumweta.
36 Wakumweta alandira kulipira, nasonkhanitsira cobala ku moyo wosatha; kuti wofesayo akakondwere pamodzi ndi womwetayo.