37 Pakuti m'menemo conenaco ciri coona, Wofesa ndi wina, womweta ndi winanso.
38 Ine ndinatuma inu kukamweta cimene simunagwirirapo nchito: ena anagwira nchito, ndipo inu mwalowa nchito yao.
39 Ndipo m'mudzi mula anthu Asamariya ambiri anamkhulupirira iye cifukwa ca mau a mkazi, wocita umboniyo, kuti, Anandiuza ine zinthu ziri zonse ndinazicita.
40 Cifukwa cace pamene Asamariya anadza kwa iye, anamfunsa akhale nao; ndipo anakhala komweko masiku awiri.
41 Ndipo ambiri oposa anakhulupira cifukwa ca mau ace:
42 ndipo ananena kwa mkazi, kuti, Tsopano sitikhulupira cifukwa ca kulankhula kwako: pakuti tamva tokha, ndipo tidziwa kuti Mpulumutsi wa dziko lapansi ndi Iyeyu ndithu.
43 Koma atapita masiku awiriwo anacoka komweko kunka ku Galileya.