1 Zitapita izi anacoka Yesu kunka ku tsidya lija la nyanja ya Galileya, ndiyo ya Tiberiya,
2 Ndipo khamu lalikuru la anthu linamtsata iye, cifukwa anaona zizindikilo zimene anacita pa odwala.
3 Koma Yesu anakwera kuphiri, nakhala pansi komweko pamodzi ndi akuphunzira ace.
4 Ndipo Paskha, phwando la Ayuda, anayandikira.