43 Yesu anayankha nati kwa iwo, Musang'ung'udze winandi mnzace.
44 Kulibe mmodzi akhoza kudza kwa Ine koma ngati Atate wondituma Ine amkoka iye; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomariza.
45 Calembedwa mwa aneneri, Ndipo adzakhala onse ophunzitsidwa ndi Mulungu. 1 Yense amene adamva kwa Atate, naphunzira, adza kwa Ine.
46 2 Sikuti munthu wina waona Atate, koma 3 iye amene ali wocokera kwa Mulungu, ameneyo waona Atate.
47 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, 4 iye wokhuluplra ali nao moyo wosatha.
48 5 Ine ndine mkate wamoyo,
49 6 Makolo anu adadya m'cipululu, ndipo adamwalira.