47 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, 4 iye wokhuluplra ali nao moyo wosatha.
48 5 Ine ndine mkate wamoyo,
49 6 Makolo anu adadya m'cipululu, ndipo adamwalira.
50 7 Mkate wotsika Kumwamba ndi uwu, kuti munthu akadyeko ndi kusamwalira.
51 8 Mkate wamoyo wotsika Kumwamba Ndine amene. Ngati munthu wina akadyako mkate umene, adzakhala ndi moyo kosatha. Inde, ndipo 9 mkate umene ndidzapatsa Ine, ndiwo thupi langa, ukhale moyo wa dziko lapansi.
52 Pamenepo Ayuda anatetana wina ndi mnzace ndi kunena, Akhoza bwanji ameneyu kutipatsa ife kudya thupi lace?
53 Cifukwa cace Yesu anati kwa iwo, Indetu, indetu, ndinenandi inu, 10 Ngati simukudya thupi la Mwana wa munthu ndi kumwa mwazi wace, mulibe moyo mwa inu nokha.