50 7 Mkate wotsika Kumwamba ndi uwu, kuti munthu akadyeko ndi kusamwalira.
51 8 Mkate wamoyo wotsika Kumwamba Ndine amene. Ngati munthu wina akadyako mkate umene, adzakhala ndi moyo kosatha. Inde, ndipo 9 mkate umene ndidzapatsa Ine, ndiwo thupi langa, ukhale moyo wa dziko lapansi.
52 Pamenepo Ayuda anatetana wina ndi mnzace ndi kunena, Akhoza bwanji ameneyu kutipatsa ife kudya thupi lace?
53 Cifukwa cace Yesu anati kwa iwo, Indetu, indetu, ndinenandi inu, 10 Ngati simukudya thupi la Mwana wa munthu ndi kumwa mwazi wace, mulibe moyo mwa inu nokha.
54 11 Iye wakudya thupi langa ndi kumwa mwazi wanga ali nao moyo wosatha; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomariza.
55 Pakuti thupi langa ndi cakudya ndithu, ndi mwazi wanga ndi caku mwa ndithu.
56 Iye wakudya thupi langa indi kumwa mwazi wanga 12 akhala mwa Ine ndi Ine mwa iye.