45 Pamenepo anyamatawo anadza kwa ansembe akulu ndi Afarisi; ndipo iwowa anati kwa iwo, Simunamtenga iye bwanji?
46 Anyamatawo anayankha, 7 Nthawi yonse palibe munthu analankhula cotero.
47 Pamenepo Afarisi anayankha iwo, Kodi mwasokeretsedwa inunso?
48 8 Kodi wina wa akuru anakhulupirira iye, kapena wa Afarisi?
49 Koma khamu ili losadziwa cilamulo, likhala lotembereredwa.
50 9 Nikodemo ananena kwa iwo, amene uja adadza kwa iye kale, ali mmodzi wa iwo,
51 Kodi cilamulo cathu ciweruza munthu, osayamba kumva iye, ndi kuzindikira cimene, acita?