12 Ndipo Davide anati kwa Uriya, Utsotse pane leronso, ndipo mawa ndidzakulola umuke, Comweco Uriya anakhala ku Yerusalemu tsiku lomwelo ndi m'mawa mwace.
13 Ndipo pakumuitana Davide, iyeyo anadya namwa pamaso pace; Davide namledzeretsa; ndipo usiku anaturuka kukagona pa kama wace pamodzi ndi anyamata a mbuye wace; koma sanatsildra ku nyumba yace.
14 Ndipo m'mawa Davide analembera Yoabu kalata, wopita nave Uriya.
15 Ndi m'kalatamo analemba kuti, Mumuike Uriya pa msongwe wa nkhondo yolimba, ndipo mumlekerere kuti akanthidwe nafe.
16 Ndipo Yoabu atayang'anira mudziwo, anaika Uriye pomwe anadziwa kuti pali ngwazi.
17 Ndipo akumudziwo anaturuka, namenyana ndi Yoabu; ndipo adagwapo anthu ena, ndiwo a anyamata a Davide; ndi Uriya Mhiti anafanso.
18 Pamenepo Yoabu anatumiza munthu nauza Davide zonse za nkhondoyi;