1 Ndipo kunali citapita ici, popeza Abisalomu mwana wa Davide anali naye mlongo wace wokongola, dzina lace ndiye Tamara, Amnoni mwana wa Davide anamkonda iye.
2 Ndipo Amnoni anapsinjikadi nayamba kudwala cifukwa ca mlongo wace Tamara, pakuti anali namwali, ndipo Amnoni anaciyesa capatali kumcitira kanthu.
3 Koma Amnoni anali ndi bwenzi lace, dzina lace ndiye Jonadabu, mwana wa Sineya, mbale wa Davide. Ndipo Jonadabu anali munthu wocenjera ndithu.
4 Nanena naye, Iwe mwana wa mfumu, uonderanji tsiku ndi tsiku? Sungandiuze kodi? Ndipo Amnoni anati kwa iye, Ndikonda Tamara, mlongo wa mbale wanga Abisalomu.