1 Ndipo Yoabu mwana wa Zeruya anazindikira kuti mtima wa mfumu unalunjika kwa Abisalomu.
2 Ndipo Yoabu anatumiza ku Tekowa, natenga kumeneko mkazi wanzeru, nanena naye, Ukokomezeke monga mfedwa, nubvale zobvala za pamaliro, osadzola mafuta, koma ukhale ngati munthu wamkazi wakulira akufa nthawi yaikuru.
3 Nulowe kwa mfumu, nulankhule nayo monga momwemo. Comweco Yoabu anampangira mau.
4 Ndipo pamene mkazi wa ku Tekowayo anati alankhule ndi mfumuyo, anagwa nkhope yace pansi namlambira, nati, Ndithandizeni mfumu.
5 Ndipo mfumuyo inanena naye, Usowanji? iye nayankha, Zoonadi ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga ana mwalira.
6 Ndipo mdzakazi wanu ndinali nao ana amuna awiri, ndipo awiriwa analimbana kumunda, panaboo wina wakuwaletsa, koma wina anakantha mnzace namupha.