34 Koma Barizilai ananena ndi mfumu, Masiku a zaka za moyo wanga ndiwo angati, kuti ndiyenera kukwera ndi mfumu kumka ku Yerusalemu?
35 Lero ndiri nazo zaka makumi asanu ndi atatu; kodi ndikhoza kuzindikiranso kusiyanitsa zabwino ndi zoipa? Mnyamata wanu ndikhoza kodi kuzindikira cimene ndidya kapena kumwa? Kodi ndikhozanso kumva mau a amuna ndi akazi oyimba? Cifukwa ninji tsono mnyamata wanu ndidzakhalanso wolemetsa mbuye wanga mfumu.
36 Mnyamata wanu angofuna kuoloka Yordano pamodzi ndi mfumu; ndipo afuniranji mfumu kundibwezerapo mphothoyotere?
37 Mulole mnyamata wanu ndibwererenso, kuti ndikamwalire m'mudzi wanga ku manda a atate wanga ndi mai wanga. Koma suyu, Cimamu mnyamata wanu, iye aoloke pamodzi ndi mbuye wanga mfumu, ndipo mumcitire cimene cikukomerani.
38 Ndipo mfumu inayankha, Cimamu adzaoloka nane, ndipo ndidzamcitira cimene cikukomereni; ndipo ciri conse mukadzapempha kwa ine ndidzakucitirani inu.
39 Ndipo anthu onse anaoloka Yordano, ndi mfumu yomwe inaoloka; ndipo mfumuyo Inapsompsona Barizilai nimdalitsa; ndipo iye anabwerera kunka kumalo kwace.
40 Comweco mfumu inaoloka nifika ku Giligala, ndi Cimamu anaoloka naye, ndipo anthu onse a Yuda adaolotsa mfumu, ndiponso gawo lina la anthu a Israyeli.