8 Koma Abineri, mwana wa Neri, kazembe wa khamu la ankhondo a Sauli anatenga Isiboseti mwana wa Sauli, namuolotsa nanka naye ku Mahanaimu;
9 namlonga ufumu wa pa Gileadi ndi Aasuri ndi Jezreeli ndi Efraimu ndi Benjamini ndi Aisrayeli onse.
10 Ndipo Isiboseti mwana wa Sauli anali ndi zaka makumi anai pakuyamba iye kukhala mfumu ya Israyeli, nacita ufumu zaka ziwiri. Koma a nyumba ya Yuda anatsata Davide.
11 Ndipo Davide anali mfumu ya nyumba ya Yuda ku Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri kudza miyezi isanu ndi umodzi.
12 Ndipo Abineri mwana wa Neri ndi anyamata a Isiboseti mwana wa Sauli anaturuka ku Mahanaimu kunka ku Gibeoni.
13 Ndi Yoabu mwana wa Zeruya, ndi anyamata a Davide anaturuka nakomana nao pa thamanda la Gibeoni; nakhala pansi, ena tsidya lino, ndi ena tsidya lija la thamandalo.
14 Ndipo Abineri ananena ndi Yoabu, Aimirire anyamata nasewere pamaso pathu. Nati Yoabu, Aimirire.