32 Ndipo Gideoni mwana wa Yoasi anafa atakalamba bwino, naikidwa m'manda a Yoasi atate wace, m'Ofira wa Aabiezeri.
33 Ndipo kunali, atafa Gideoni, ana a Israyeli anabwereranso nagwadira Abaala, nayesa Baala-beriti mulungu wao.
34 Ndi ana a Israyeli sanakumbukila Yehova Mulungu wao, amene anawapulumutsa m'dzanja la adani ao onse pozungulira ponse;
35 osacitira cifundo nyumba ya Yerubaala, ndiye Gideoni, monga mwa zokoma zonse iye anacitira Israyeli.