Oweruza 12 BL92

Efraimu aukira Yefita

1 Pamenepo amuna a Efraimu analalikidwa, napita kumpoto; nati kwa Yefita, Wapitiriraoji kuthira nkhondo ana a Amoni, osatiitana ife timuke nawe? Tidzakutenthera nyumba yako ndimotopamtupako.

2 Ndipo Yefita anati kwa iwo, Ine ndi anthu anga tinatsutsana kwakukuru ndi ana a Amoni, koma pamene ndinakuitanani inu simunandipulumutsa m'dzanju lao.

3 Ndipo pakuona ine kuti simunandipulumutsa, ndinataya moyo wanga ndi kupita kwa ana a Amoni; ndipo Yehova anawapereka m'dzanja langa; mwakwereranji tsono lero lino kundicitira nkhondo?

4 Pamenepo Yefita anamemeza amuna onse a m'Gileadi nalimbana naye Efraimu; ndipo amuna a Gileadi anakantha Efraimu, cifukwa adati, Inu Agileadi ndinu akuthawa Efraimu, pakati pa Efraimu ndi pakati pa Manase.

5 Ndipo Agileadi anatsekereza madooko a Yordano a Efraimu; ndipo kunatero kuti, akati othawa a Efraimu, Ndioloke, amuna a Gileadi anati kwa iye, Ndiwe M-efraimu kodi? Akati, Iai;

6 pamenepo anati kwa iye, Unene tsono Shiboleti; ndipo akati, Siboleti, osakhoza kuchula bwino, amgwira namupha padooko pomwe pa Yordano; ndipo anagwa a Efraimu nthawi ija, zikwi makumi anai mphambu ziwiri.

7 Ndipo Yefita anaweruza Israyeli zaka zisanu ndi cimodzi; nafa Yefita Mgileadi, naikidwa m'mudzi wina wa Gileadi.

Oweruza Ibzani, Eloni, Abidoni

8 Ndi pambuyo pace Ibzani wa ku Betelehemu anaweruza Israyeli.

9 Ndipo anali nao ana amuna makumi atatu; ndi ana akazi makumi atatu anawakwatitsa kwina, natengera ana ace amuna ana akazi makumi atatu ocokera kwina. Ndipo anaweruza Israyeli zaka zisanu ndi ziwiri.

10 Nafa Ibzani naikidwa ku Betelehemu.

11 Ndi pambuyo pace Eloni Mzebuloni anaweruza Israyeli; naweruza Israyeli zaka khumi.

12 Nafa Eloni Mzebuloni naikidwa m'Aijaloni m'dziko la Zebuloni.

13 Ndi pambuyo pace Abidonf mwana wa Hilele wa ku Piratoni anaweruza Israyeli.

14 Ndipo anali nao ana amuna makumi anai ndi zidzukulu zazimuna makumi atatu, akuyenda okwera pa ana a aburu makumi asanu ndi awiri; naweruza Israyeli zaka zisanu ndi zitatu.

15 Nafa Abidoni mwana wa Hilele wa ku Piratoni, naikidwa m'Piratoni m'dziko la Efraimu ku mapiri a Amaleki.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21