16 Ndipo anawasonkhanitsira ku malo ochedwa m'Cihebri Harmagedo.
17 Ndipo wacisanu ndi ciwiri anatsanulira mbale yace mumlengalenga; ndipo m'Kacisimo mudaturuka mau akuru, ocokera ku mpando wacifumu ndi kunena, Cacitika;
18 ndipo panakhala mphezi, ndi mau, ndi mabingu; ndipo panali 1 cibvomezi cacikuru cotero sicinaoneke ciyambire anthu padziko, cibvomezi colimba cotero, cacikuru cotero.
19 Ndipo 2 cimudzi cacikuruco cidagawika patatu, ndi midzi ya amitundu inagwa; ndipo 3 Babulo waukuru unakumbukika pamaso pa Mulungu, kuti aupatse cikho ca vinyo wamkali wa mkwiyo wace.
20 Ndipo 4 zisumbu zonse zidathawa, ndi mapiri sanapezeka.
21 Ndipo 5 anatsika kumwamba matalala akuru, lonse lolemera ngati talenti, nagwa pa anthu; ndipo anthu 6 anacitira Mulungu mwano cifukwa ca mliri wa matalala, pakuti m1iri wace nm waukuru ndithu.