11 Ndipo ndinaona mutatseguka m'Mwamba; ndipo taonani, kavalo woyera, ndi iye wakumkwera wochedwa Wokhulupirika ndi Woona; ndipo aweruza, nacita nkhondo molungama.
12 Ndipo maso ace ali lawi la moto, ndi pamutu pace pali nduwira zacifumu zambiri; ndipo ali nalo dzina lolembedwa, wosalidziwa wina yense koma iye yekha.
13 Ndipo abvala cobvala cowazidwa mwazi; ndipo achedwa dzina lace, Mau a Mulungu.
14 Ndipo magulu a nkhondo okhala m'Mwamba anamtsata iye, okwera pa akavalo oyera, obvala bafuta woyera woti mbu.
15 Ndipo m'kamwa mwace muturuka Iupanga lakuthwa, kuti akanthe nalo mitundu ya anthu; ndipo iye adzawalamulira ndi ndodo yacitsulo: ndipo aponda iye moponderamo mphesa mwa vinyo waukali wa mkwiyo wa Mulungu Wamphamvuyonse.
16 Ndipo ali nalo pa cobvala cace ndi pa ncafu yace dzina lolembedwa, MFUMU YA MAFUMU, NDI MBUYE WA AMBUYE.
17 Ndipo ndinaona mngelo alikuima m'dzuwa; ndipo anapfuula ndi mau akuru alrunena 1 ndi mbalame zonse zakuuluka pakati pa mlengalenga: 2 Idzani kuno, sonkhanani ku phwando la Mulungu wamkuru,