24 Koma ndinena kwa inu, kwa otsala a ku Tiyatira, onse amene alibe ciphunzitso ici, amene sanazindikira zakuya za Satana, monga anena, Sindikusanjikizani katundu wina.
25 Koma 5 cimene muli naco, gwirani kufikira ndikadza.
26 Ndipo iye amene alakika, ndi iye amene asunga nchito zanga kufikira citsiriziro, kwa iye 6 ndidzapatsa ulamuliro wa pa amitundu;
27 ndipo 7 adzawalamulira ndi ndodo yacitsulo, monga zotengera za woumba mbiya ziphwanyika mapale; monga lnenso ndalandira kwa Atate wanga;
28 ndipo ndidzampatsa iye 8 nthanda.
29 Iye wokhala nalo khutu amve cimene Mzimu anena kwa Mipingo.