10 Koma ansembe akulu anapangana kuti akaphe Lazaronso;
11 pakuti ambiri a Ayuda anacoka cifukwa ca iye, nakhulupirira Yesu.
12 M'mawa mwace khamu lalikuru la anthu amene adadza kuphwando, pakumva kuti Yesu alinkudza ku Yerusalemu,
13 anatenga makwata a kanjedza, naturuka kukakomana ndi iye, napfuula, Hosana; wolemekezeka iye wakudza m'dzina la Ambuye, ndiye Mfumu ya Israyeli.
14 Koma Yesu, m'mene adapeza kaburu anakhala pamenepo; monga mulembedwa:
15 Usaope, mwana wamkazi wa Ziyoni; taona Mfumu yako idza wokhala pa mwana wa buru.
16 Izisanazidziwa aku phunzira ace poyamba; koma pamene Yesu analemekezedwa, pamenepo anakumbukila kuti izi zinalembedwa za iye, ndi kuti adamcitira iye izi.