23 Ndipo tsiku limenelo simudzandifunsa kanthu. Indetu, indetu, ndinena kwa inu, Ngati mudzapempha Atate kanthu, adzakupatsani inu m'dzina langa.
24 Kufikira tsopano simunapempha kanthu m'dzina langa; pemphani, ndipo mudzalandira, kuti cimwemwe canu cikwaniridwe.
25 Zinthu izi ndalankhula ndi inu m'mafanizo; ikudza nthawi imene sindidzalankhula ndi inu m'mafanizo, koma ndidzakulalikirani inu momveka za Atate.
26 Tsiku limenelo mudzapempha m'dzina langa; ndipo sindinena kwa inu kuti Ine ndidzafunsira inu kwa Atate;
27 pakuti Atate yekha akonda inu, cifukwa inu mwandikonda Ine, ndi kukhulupirira kuti Ine ndinaturuka kwa Atate.
28 Ndinaturuka mwa Atate, ndipo ndadza ku dziko lapansi: ndilisiyanso dziko lapansi, ndipo ndipita kwa Atate.
29 Akuphunzira ace ananena, Onani, tsopano mulankhula zomveka, ndipo mulibe kunena ciphiphiritso,